1 Atesalonika 5:1-28 OCCL
[1] Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni, [2] chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku. [3] Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa. [4] Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala. [5] Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima. [6] Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga. [7] Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku. [8] Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa. [9] Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. [10] Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi. [11] Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira. [12] Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani. [13] Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake. [14] Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense. [15] Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse. [16] Kondwerani nthawi zonse. [17] Pempherani kosalekeza. [18] Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu. [19] Musazimitse moto wa Mzimu Woyera. [20] Musanyoze mawu a uneneri. [21] Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino. [22] Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse. [23] Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu. [24] Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi. [25] Abale, mutipempherere. [26] Perekani moni wachikondi kwa onse. [27] Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse. [28] Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.
